Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 202

Miyambi ya Patsokwe chochita.” Pafera kambuku pali matatalazi. -Pamene pagonja wamphamvu kwambiri pali mavuto. Pafera munthu salephera kudzumapo. -Munthu mavuto akamupanikiza amadzuma ndipo ena amamva n’kumuthandiza. Pafuka utsi pali moto. -Mphekesera iliyonse imakhala ndi nkhanikhani. Pafupi ndi apo wafika. -Osamadalira zinthu zomwe sunapeze. Ndi bwino kumathokoza zimene uli nazo. Pafupi padaolera njovu. -Njovu itafa anthu ankati ili pafupi koma kuli kutali moti mpaka njovuyo inaola anthu asanapiteko. Ukamafuna kugwira ntchito, ngakhale yaing’ono, umafunika kukonzekera bwino kuti uimal- ize m’malo momangoiderera. Pagona tonde padzinunkha. -Munthu aliyense ayenera kuchita khama pantchito kuti padzioneka kuti panali munthu. Pagule fumbi ndiwe mwini. -Munthu aliyense amalimbikira kuchita zinthu zake. Amaonet- setsa kuti zachitika bwino kwambiri koposa mmene akanachitira za ena. Pagwa fisi paterera. -Pamene munthu wamkulu walakwa ndiye kuti panavuta. Pakadafunda padajiwitsa galu. -Tsiku lina galu anagona penapake pamene pamkamveka bee, moti mpaka analephera kukalowa m’nyumba ndipo anagona pomwepo. Fisi atabwera anangomutola. Kukakamira kuchita 201