Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 189
Miyambi ya Patsokwe
Nkhuyu zodya mwana zidapota akulu.
-Nthawi zambiri ana akapalamula vuto lonse limafikira kwa ma-
kolo ndipo makolowo ndi amene amavutika nalo.
Nkhwangwa ikati chubwi m’madzi, dzanja lako lipite pom-
wepo.
-Tisamazengereze kuchita zinthu. Mavuto kapena zina zikachi-
tika, ndi bwino kuchitiratu chifukwa tikachita ulesi zikhoza
kutisokonekera.
Nkhwangwa imakhulupirira mpini.
-Anthu amayenera kukhulupirirana komanso kuthandzana kuti
zinthu ziyende.
Nkhwangwa siithwera pachipala.
-Munthu samaphunzira zonse kusukulu, kuchinamwali kapena
kwa makolo ake. Amatha kuphunzira zina akamachita zinthu
ndi anthu ena.
Nkhwangwa yatema bondo.
-Nkhwangwa yako ikakutema sumaiwala. M’bale wako akaku-
lakwira ndi bwino kumukhululukira m’malo momangosunga
chakukhosi.
Nkhwangwa yobwereka siichedwa kuguluka.
-Munthu sachedwa kuchita ngozi ndi chinthu chobwereka.
Nkhwangwa yobwereka sichedwa kusweka mpini.
-Munthu sachedwa kuchita ngozi ndi chinthu chobwereka.
Nkhwangwa yobwereka siichedwa kuthyoka.
-Zinthu zobwereka sizikhalitsa, umafunika kupeza zako.
Nkhwani saotchera.
-Mawuwa anganenedwe ngati wina wachita zinthu zabwino
kwambiri moti sitingachitirenso mwina koma kumuyamikira.
Anganenedwenso ngati wina akuyesa kuchita zosatheka.
188