Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 179
Miyambi ya Patsokwe
Ndam’meta mpala wopanda madzi.
-Munthu amanena mawuwa potanthauza kuti wamuchenjeretsa
winawake kapena wamukhaulitsa.
Ndangotsala madzi amodzi.
-Mawuwa amatanthauza kuti ndangotsala pang’ono kufa.
Ndani amene angaike khala lamoto pamalaya ake koma
osapsa?
-Palibe munthu amene angachite choipa osakumana ndi zotsati-
ra zake.
Ndapakonda adasiya khonde.
-Kuzengereza pochita zinthu kumapezetsa mavuto.
Ndaphwa mafuta, patsala thonje lokha.
-Mawuwa amatanthauza kuti munthu ali ndi njala. Kuphwa ma-
futa akutanthauza kuti wapuma koma akumva njala.
Ndawonera momwemu mwambi wa gulugufe.
-Ndi bwino kumakhutitsidwa ndi zimene uli nazo ngakhale zili
zochepa.
Ndayala mayani, awuma.
-Ndadikira mokwanira moti ndatopa.
Ndewonetsetse adathetsa nkhosa.
-Kuzengereza kumagwetsera munthu m’mavuto.
Ndewu siimanga mudzi.
-Mikangano komanso ndewu zimapasula mudzi. M’malo mo-
chita zimenezi ndi bwino kukambirana mwamtendere.
Ndi bwino kunena maganizo ako udakali ndi moyo, kusiyana
n’kumadzawanena ukutsirizika.
-Osamamangika kunena maganizo ako chifukwa mwina
angathandize.
178