Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 177

Miyambi ya Patsokwe N’takalamba n’kusiya dziko likali nsonga. -Mawuwa amanenedwa munthu akamafuna kunena kuti akufu- na kuchoka zinthu zikadali bwino, pamalo pasanaipe. Nachonso chitsiru chili ndi mwini. -Munthu ngakhale wopusa amakhala ndi m’bale wake amene amamukonda. Akaphedwa abale ake adzaoneka. Choncho si bwino kunyoza ena chifukwa cha khalidwe kapena maon- ekedwe awo. Nalikukuti saluma, koma akaluma alibe chivumulo. -Pali anthu ena omwe amaoneka a phee, koma tsiku lina ukadzawaputa umadzaona kuti ali ndi ululu woopsa kuposa wa njoka. Namkwichi akaona akazi ndiye amakondwa. -Namkwichi ndi mbalame yokonda akazi kwambiri. Mwam- biwu umanena za munthu wokonda akazi. Nankholowa ali m’manja n’kulinga utalawa. -Pali njira zosiyanasiyana zophikira nankholowa (masamba a mbatata). Tisamaweruze nsanga chinthu tisakuchidziwa bwino. Nankungwi chilanga anzake, mwake sazira. -Pali anthu ena omwe amakonda kulangiza anzawo pomwe iwowo sachita zimenezo, kapena alibiretu khalidwe. Nankununkha sadzimva. -N’kovuta kuti munthu adziwe za momwe anthu ena amamuon- era makhalidwe ndi maonekedwe ake, koma anthu enawo ndi- wo amamudziwa bwino. Nanzeze apitira m’kuleza. -Timanena mawu amenewa munthu akawomboka pamavuto amene anawapeza kuchokera kwa anthu amene sanamvetse bwino nkhani yonse. Ngati Nanzeze yemwe anapulumuka 176