Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 165

Miyambi ya Patsokwe Munthu wopanda maso samunamiza maso. -Tisamalonjeze zinthu zomwe sitingakwanitse kuchita, monga kuchititsa kuti wakhungu aone. Munthu wopata safa ndi chuma. -Munthu akamwalira samatenga chuma kumanda. Choncho ngakhale tilemere, si bwino kumayerekedwa chifukwa ndalama sizingatiike m’manda. Munthu wosabala amasowa chomutukwanira mwamuna. -Mayi amene ali ndi mwana amatha kum’tukwana mwana wake pamene wayambana ndi mwamuna wake. Akakhala wopanda mwana amasowa womutukwana. Munthu wosauka sapha nyama ya nguwo. -Munthu umayenera kufufuza zinthu mogwirizana ndi mmene umapezera zinthu. Osamafuna zinthu zomwe sungathe kuzipe- za. Munthu wotolatola samera ndevu zoyera. -Munthu wamakhalidwe oipa sakalamba. Musade Vumbwe, akudya nkhukhu ndi Kalulu. -Nthawi zambiri pamudzi pakachitika zoipa amaganiza kuti mdani wawo ndi amene wawachitira zimenezo. Koma nthawi zina anthu omwe amaoneka ngati Akalulu ndi amene amakhala atachita zoipazo. Musamati ndi masweswe lili dazi. -Si bwino kumanyozera zinthu anthu ena akamanena. Musamati ndikuthawa mlomo, mlomo uli kulikonse. -Kuthawa mlomo ndi kuthawa kulongolola. Mavuto ali ponseponse ndipo sitingawathawe. Amene akufuna kuwathawa kuli bwino angomwalira. 164