Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 160

Miyambi ya Patsokwe kwa iwo basi, ngati mmene munthu amakwerera mumtengo kuti akangothyola mango basi. Mtengo wopanda tsinde mudauonapo? -Ngati tikufuna kuona khalidwe la ana ndi bwino tiyang’ane makolo awo. Kuti umvetse zochita za munthu wina ndi bwino kufufuza mbiri yake. Mthamangira kuotha anasiya moto ukuyaka. -Munthu wothamangira kuchita zinthu ndi amene amayambiri- ra kukumana ndi mavuto. Ndiye anzake amabwera n’kudzape- za zabwino, apo ayi amaphunzirira pa tsoka lakelo. Mthanga kunena adapisa Likongwe wa apongozi. -Mwambiwu umanena za mkamwini wina yemwe anafulumira kapena kuti kuthanga kunena kuti amene atathawitse Likongwe asamuka pamudzi. Ndiye zinachitika kuti iyeyo ndi amene anathawitsa Likongweyo ndipo zinamuvuta. Tisamalonjeze msanga za chinthu chomwe sitikudziwa kuti chitha bwanji. Mtima suvala nsanza. -Munthu akhoza kukhala wosauka, koma mumtima mwake n’kukhala wolemera kwambiri pa zimene amakhumba. Palibe amalota ali wosauka. Mtima uli ngwizi, kadziwe ka mu Likuni. -Mwambiwu umanenedwa pofuna kutanthauza kuti wakwiya kwambiri, uli ndi nkwiyo wosaneneka. Mtima ulikuperewera, chanka patali. -Ngati mtima sukhumbira chinachake ndiye kuti n’zosatheka kuchipeza. Mtima wabwino ngwaumulungu. -Munthu wamtima wabwino amachitanso zabwino. 159