Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 156

Miyambi ya Patsokwe Mphepo yakumpoto indachititsa mkamwini kuba m’munda mwa apongozi. -Umphawi kapena mavuto ena chisamakhale chifukwa chochitira zoipa monga kuba, kutukwana ndi zina. Mphini yobwereza ndi imene imawala. -Malangizo obwereza ndi amene amamveka bwino. Mphongo ya Chiwala sichepa. -Si bwino kunyoza amuna kapena akazi a ena chifukwa ndi amuna kapena akazi awo basi. Mphongo zidana. -Nthawi zambiri amuna sachitira amuna anzawo zabwino. Ko- ma akakhala mkazi amatha kumuchira zabwino kwambiri. Mphungu sataya nthenga. -Mawuwa amanena za munthu woumira. Mphungu ndi mbalame imene imauluka m’mwamba kwambiri, koma ikag- wetsa nthenga, imawakha mthengayo isanafike pansi. Mphuno imodzi silowa zala ziwiri. -Si bwino kuchita zinthu ziwiri nthawi imodzi chifukwa nthawi zina umatha kulephera kukwaniritsa zonsezo. Mphuno salota, adawombera mfiti m’manja. -Munthu woipa kapena wabwino alibe fungo. Nthawi zina ame- ne timawaona ngati abwino ndi amene amadzatipha. Ukhoza kuchitira zabwino munthu amene angadzakunyoze patsogolo. Mphwanga ndiye wamkulu msinkhu, ngakhale kuti ndi- natsogola ndine. -Kukhala ndi mnzeru si kubadwa kale kapena kutalika. Mphwanga, mukakula bwino ngati mwana wa Mlamba. -Ndi bwino kumakhala wochenjera ndiponso kumakhala bwino 155