Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 151

Miyambi ya Patsokwe ndi mafunso ndiye akusowa choyankha. Mluzu wa agalu ndi umodzi. -Munthu wanzeru sadikira kuti amve uthenga wakewake. Pa zo- chitika zina monga maliro kapena msonkhano timafunika ku- chita zinthu mofulumira komanso mogwirizana. Mmene ndalimira ndi msana wanga sindingalephere kudyapo. -Munthu amayenera kusangalala ndi ntchito imene wagwira ko- manso zimene wazivutikira kuti azipeze. Mnyanga sulemera mwini. -Ana kapena abale ako ngakhale atakhala ovuta kapena olumala timafunika tisatope nawo chifukwa amadalira ifeyo basi. Mnzako akakuchenjeretsa pogona, iwe umuchenjerere podzu- ka. -Ngati mnzako ali ndi luso linalake lomwe iwe ulibe, uyenera kulimbikira zimene umachita bwino kuposa iyeyo. Mnzako akakutema mphini kumbuyo, iwenso umuteme kum- buyo. -Mnzathu akatithandiza, ndi bwino kudzamuthandizanso akadzavutika m’malo mobweza chipongwe. Mnzako akakuti konzu, nawe umam’ti konzu. -Mnzako akukuchitira zabwino nawenso ndi bwino kumuchitira zabwino. Mnzako akapsa ndevu m’zimire. -Tizithandiza anzathu akakhala pamavuto chifukwa tsiku lina tidzawafuna. Mnzako akapsa ndevu mzimitse, mawa adzazimitsa zako. -Mnzako akakhala pamavuto muthandize chifukwa mawa akho- za kudzakuthandiza iweyo. 150