Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 114

Miyambi ya Patsokwe Kwa eni uyenda umayeteka. -Kuchilendo sukhala ndi ufulu wochita kapena kuyankhula chil- ichonse chimene ukufuna. Kwa eni, kapitolosi umaika m’kamwa. -Munthu ukakhala kwa eni umakhala opanda ufulu wochika kapena kuyankhula chilichonse chimene ukufuna. Tiyenera ku- khala odzichepetsa tikhala kwa eni. Kapitolosi ndi ndevu za pamlomo. Kwafa galu kulibe mbiri. -Munthu wosadziwika akalakwa, choipa chake sichidziwika kwambiri. Munthu wodziwika akalakwa, mbiri imapita patali. Kwagwa chauta. -Mawuwa amanenedwa kukachitika mliri womwe wapulula an- thu ambiri kapena kukachitika maliro. Kwagwera mtengo wanthambi sikusowa. -Anthu otchuka akalakwa mbiri imafala kwambiri, koma osatch- uka nkhani yake sidziwika kwenikweni. Kwakuchera uname. -Pali anthu ena omwe kukangocha ntchito imakhala kunena miseche. Ukanena zabodza suchedwa kugwidwa. Kwakula kometa, waperewera kundwe (pawudala). -Pogwira ntchito pamafunika anthu okwanira. Mawuwa amanenedwa ikakhala kuti ntchito ndi yambiri koma anthu ndi ochepa. Kwalusa n’kulinga wina atajiwa. -Timachenjera kwambiri pavuto ngati wina zamuonekera. Kwanu n’kwanu, m’nthengo mudalaka njoka. -Osamanyoza kwanu chifukwa zinthu zikakuvuta umabwerera kwanu. 113