Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 98
Matigari
“Ndine wogwira ntchito,” anaitokosa motero. “Ndakhala
ndikugwira ntchito pafakitale imene ija kwa zaka zosawerenge-
ka ndipo zimene Matigari wanena ndi choonadi chokhachokha.
Ndakhala ndikugwira ntchito mokhulupirika kwa moyo wanga
wonse. Koma tangoonani mmene mashini ayamwira mphamvu
zanga. Mashini asungunula minofu yanga yonse moti ndan-
gotsala mafupa okhaokha. N’chifukwa chaketu ndikungooneka
ngati nzukwa. Thupi langa likungoyoyoka ngakhale ndiku-
madzilimbitsabe mtima kuti zidzayenda. Ndakhala ndikuziuza
kuti: ‘Munthu wolimbikira savutikiratu; munthu wopirira ama-
pambana; anamwa tiyi adzamwanso, bola osataya masipuni.’
Koma kodi ndidzatsala ndi chiyani ndikadzapuma pantchito?
Adzangondipatsa nsalu pothokoza chintchito chonse chomwe
ndakhala ndikugwira mokhulupirika kwa zaka zonsezi. Zoona
kugwira ntchito zaka zonsezi koma osalandira penshoni. Kodi
mukudziwa? Ndakhala zaka zonsezi ndisakunyanyala nawo
ntchito kapena kuchita ziwonetsero zosonyeza kusagwirizana
ndi kuchepa kwa malipiro. Ndinkadziuza kuti: ‘Ndikachita na-
wo zimenezi n’kundichotsa ntchito, ndipeza kuti ndalama zo-
gulira chakudya cha ana anga?’ Koma taonani tsopano.
Ndamangidwatu popanda chifukwa n’chimodzi chomwe. Ndiye
mwina mukufunsa kuti ndiye ndabwereranji kuno? Dikirani
ndikuuzeni.”
“Masanawa, ndimayenda mphepete mwa nsewu n’kumapita
kunyumba kwanga. Ndimadziuza kuti: ‘Bola ndisiyire kunyan-
yala ntchitoku anthu ochenjera mopusawa, ndiwasiye akumvet-
sera anthu ankamwa mwakukha uchi ngati Ngaruro wa Kiriro.’
Munthu wina wamsinkhu wangawu anaima n’kundifunsa kuti:
‘Kodi mwamva zimene zachitika?’ ‘Kwachitika chiyani? Mesa
anthu akunyanyala ntchito chifukwa choti malipiro achepa?’
97