Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 92

Matigari Palibenso chikondi chotere, pakati pa amayi ndi ana. Choti nyemba ikagwera pansi, amagawana n'kudya limodzi. Tiyeni tonse tigawane nyemba imodziyi, komanso kamowa kali m'botoloka.” Pali chinachake chomwe chinali m'mawu a Matigari chomwe chinachititsa onse kuyamba kumumvetsera mwatcheru. Mawu akewo anali achifundo, komanso anali ndi mfundo zopatsa chiyembekezo ndi chilimbikitso. Ena onse aja anangokhala duu n’kumamvetsera. Mawu akewa anawakumbutsa zinthu zomwe anali ataziiwala, zinawakumbutsa za maloto omwe anali nawo kalekalero. “Ndiye tiona bwanji mumdima ngati umenewu?” Uja anag- widwa akungoyendayenda m'tauni uja anafunsa. “Palibe amene amaphonya pakamwa pake!” Uja ankaim- bidwa mlandu wopha munthu uja anatero. “Nanga bwanji chakudya china chitagwera pankodzo,” uja anagwidwa akufuna kuba kachikwama uja anatero. “Mwinanso chikhoza kugwera pamasanzi,” wakuba nsima uja anawonjezera. “Basi, masanzi komanso mkodzowo ukhoza kungosanduka supu wathu,” mwana wakuyunivesite uja ananena moseleula. “Utisanzitsa iwe!” anagwidwa ndi mlandu woyendayenda uja anatero moipidwa. “Sukudziwa kuti mitima ya enafe sichedwa kuyamba kuyendayenda?” “Komanso enafe mutithawitsira chilakolako choti tidye,” anatero ankafuna kuba kachikwama uja. 91