Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 90

Matigari Anthu ena amatha kukhalabe zitsiru ngakhale atamera ndevu. Basitu, kumene apolisi anatulukira sindinakuone. Kenako ananditsira unyolo pamlandu wochita zinthu zovutitsa. Wina anali mphunzitsi yemwe anamangidwa pamlandu wophunzitsa ziphunzitso za Marx komanso ziphunzitso zina zachikomyunizimu kusukulu. “Kodi mukudziwa chifukwa chimene akundiimbira mlandu- wu? Ati chifukwa choti ndinanena kuti mfundo zimene mayiko monga Soviet Union, China, Cuba komanso mayiko ena achikomyunizimu amayendera ndi zimene Marx ndi Lenin an- kaphunzitsa. Koma ndili ndi funso limodzi. Ngati nditalephera kuphunzitsa ana zinthu zoona, ndiye ndiziwaphunzitsa chi- yani?” Munthu wachisanu ndi chiwiri anamangidwa chifukwa anali ndi cholinga chotsomphola kachikwama kam'manja ka mayi wina wochita bwino. “Ndinaona mayi wina wotchena akuwerenga mulu wa ma 100 shilings ndipo mumtima mwanga ndinangoti: Ndalama izo zimayenera kukhala zathu. Ofunika ndizitenge kuti ndimuthan- dize kuzigwiritsa ntchito. Ndiye ndinayamba kumutsatira. Atan- gotsala pang'ono kulowa mu Mercedes-Benz, ndi . . . nanga ndi- kanadziwa bwanji kuti pafupi ndi ine panali wapolisi yemwe sa- navale yunifomu? Basitu anandimbwandira pamlandu wakuba.” Woledzera uja anamangidwa chifukwa chopezeka atamwa mowa mopitirira muyeso. “Kodi zimenezizi ndi zomveka?” anafunsa motero, “Ndikapanda kumwa mowa ndiye ndizichita chiyani ndi moyo wangawu? Pofika pano, ndi Matigari komanso anthu ena wiri omwe 89