Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 88

Matigari “Mukudziwa, nthawi zina zimene anthu oledzera amakamba zimakhala ndi kanthu kenakake kanzeru!” “N'chifukwa chake ena amati mowa ukhoza kuthandiza munthu kuzindikira zinthu zozama. Oledzera akhoza kutitsegula m’maso kuti tithe kuzindikira zinthu zofunika.” “Zimenezo ndi zoona, chifukwa zimene woledzerayu wanena ndi choonadi chenicheni. Dziko lathulidi ndi louma gwa ngati konkireti ili pansiyi. Atsogoleri athu ali ndi mitima youma ngati ya Farao. Mwinanso youma kuposa ya atsamunda aja. Iwo samva kulira kwa anthu a m'dziko lawo.” “Zimenezo ndi zoonadi, nanga mungandifotokozere bwinobwino chifukwa chake apolisiwa andimanga lero?” “Nanjinanji ine!” Kenako onse anaiwala za mkodzo wa woledzera uja ndipo anayamba kufotokozerana zimene zinachitika kuti amangidwe. Mmene ankachezera zinkangokhala ngati akhala akudziwana kwa zaka zambiri. M'modzi mwa anthuwo anali mlimi. Anali atamangidwa popezeka akugulitsa mkaka popanda chilolezo. “Linalitu botolo limodzi lenileni! Pamene ndimachokera ko- kagula makandulo kuti ndidzipita kunyumba ndinangowaona atulukira, kenako ndinangozindikira anditsira unyolo amvekere: 'Tionetseni chikalata chokulolezani kugulitsa mkaka m'tauni muno.'” Wina anamangidwa ataba nsima pamalo ena ogulitsira chakudya. “Nanga ine ndikanatani mwana wamatumbo atavuta? Ndi- nali nditatheratu ndi njala moti sindikanachitira mwina.” 87