Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 86
Matigari
Gawo 13
Matigari anaponyedwa muselo ina yamdima momwe munali
mutadzadza ndi mpweya wa anthu ena khumi omwe
analongedzedwa m'menemo. Munkamvekanso fungo lonyansa
kwambiri la masanzi a mowa, thukuta komanso magazi omwe
anapakikapakika m'makoma a seloyo kwa zaka zambiri.
Museloyo munalibe mpweya wabwino moti zinkangokhala nga-
ti awatsekera m'botolo modzadza ndi fungo loipa. Matigari
anayesetsa kuti achotse nseru yomwe inamugwira atangolowa
museloyo. Museloyo munangoti zii kupatulapo mkonono wa
chidakwa china chomwe chinali chitagona pamasanzi ake.
Kenako m'modzi mwa anthu omwe anali museloyo anakuwa
kuti: “Kodi ndi ndani amene akukodzayo?”
“Ndi woledzera wagona apayu!” anthu angapo anayankha
mogwirizana.
Anthu omwe anali museloyo anayamba kudzipanikiza ku-
khoma kuti mpope wamkodzo wa woledzerayo usawanyowetse,
koma zinali zosatheka kusuntha chifukwa anali atagunda kale
khoma. Ena anayamba kuyankhula momoipidwa kwambiri po-
funa kusonyeza kuti zimene zikuchitikazo zikuwanyansa ndipo
ena anayamba kulalata:
“Posachedwapa anasanza! Pano ndi uyu akukodzayu!”
“Kenako atinyerera ndithu!”
“Tamutsinani adzuke!”
“Tamukhomani!”
“Iwe tadzuka, wewe pund a m ilia!”* m'modzi mwa anthuwo
anamukhoma ndipo woledzerayo anadzuka.
*Wewe punda milia! (Kiswahili): kutanthauza, “Mbuzi iwe!”
85