Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 80

Matigari tinamutumiza kuti akachite maphunziro, tikumanena kuti mwa- na wanzako ndi wako yemwe, ukachenjera manja umadya naye? Tikumanyadira kuti tsogolo la dziko lathu lagona mwa mwana ameneyu, mwana yemwe adzatimenyere nkhondo yolimbana ndi atsamunda! Koma tikanadziwa tikanangokazinga ndithu! Mbewu tinadzalayi ndi chitedze chenicheni." "Tandimvetserani bwinobwino. Mzee, ndikufuna ndikupem- pheni kuti muphunzire tanthauzo la mawu akuti ‘munthu.’ Dzi- ko lathuli lakhala lili mumdima wandiweyani chifukwa cha um- buli wa anthu athu omwe sadziwa tanthauzo la mawu ame- newa. Anthu ake sadziwa kufunika kwa mawu akuti, ‘munthu,’ mosiyana ndi mawu akuti ‘chigulugulu.’ Azungu akutukuka chifukwa amazindikira tanthauzo la mawu amenewo, choncho amalemekeza ufulu wa m unthu, zimene zikutanthauza kuti munthu aliyense ali ndi ufulu wochita zimene akufuna mosasa- mala kanthu kuti ena amaziona bwanji. Chulukechuluketu ngwa njuchi. Koma anthu akudanu mumachita zinthu ngati winawake anakumangirirani banja, fuko, dziko komanso anthu amtundu wanu pamsana. Munthu wina akamafuna kuchita zinthu zomwe zingamuthandize kuti atukuke komanso apite patsogolo, mumamugwira juzi n’kumamukokera m'mbuyo. Kodi mawu akuti 'chigulu' amatanthauza chiyani? Mzee, ndikufuna ndikuuzeni kuti nkhokwe yagulu imakhala yopanda kathu. Nthawi zonse zinthu zagulu zimanyamulidwa m'chidebe chopanda matako. Chifuyo cha aliyense chimafa ndi njala. Kodi paja nyimbo ija imati chiyani? Yend a bw ino aise tio nana, ali- yense ayendere yake. Sikuti thupi langa laphukira pansama pakopo ko- manso sikuti pali amene wabereka mnzake! Bambo anga ankadziwa zimenezi, n'chifukwa chake ananditumiza kusukulu. Iwo anatseka mapirikaniro awo kuti asamve zomwe zitsiru zina zinkanena, kuti tiyenera kugawana komanso kudyera limodzi 79