Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 73

Matigari “Heyi, m zee,” * munthu wakuda uja anafuula motero. “Kodi sukuona chikwangwanicho? Hak una njia.* Ha ha ha! . . . Kapena sumatha kuwerenga? Komansotu imeneyo si njira yopita kunyumba za ogwira ntchito.” *Mzee (Kiswahili): Kutanthauza “Munthu wokalamba kapena kuti Madala.” *Hakuna njia (Kiswahili): Kutanthauza “Palibe njira.” Matigari anatembenuka, n’kuyang’ana munthu uja kwa kan- thawi, kenako anamufunsa kuti: “Kodi kumeneko n’kumene kuli makiyi?” “Makiyi a chiyani?” “Makiyi otsegulira m’nyumba.” “Nyumba yake iti?” “Iyiyi.” “Ukufuna utani nawo makiyiwo?” “Mukufunsatu chinyezi kubafa, kapena nditi fungo m’chimbudzi! Moti simukudziwa kuti makiyi timatsegulira chitseko? Ndikufuna ndikatsegulire chitseko cholowera m’nyumbayi! Ndakhala ndili koyenda kwa nthawi yaitali ndiye ndabwerako tsopano.” “Ndiye ukuganiza kuti iyiyi ndi nyumba yogona alendo?” Munthu wakuda uja anafunsa mwakachipongwepongwe ee. “Bob, tabwera udzamve zimene mdalayu akunena, eti akuti nyumbayi ndi yake!”* *Kugonekedwa kwa mawuwa kukusonyeza kuti anthuwa akuyankhulana Chingerezi osati Chigikuyu. Munthu wakuda uja tsopano anatsika pahatchi ija atagwira chingwe chokokera hatchiyo n’kumalowera kumene kunali Matigari. Mnzake uja, yemwe anali adakali pahatchi anabweran- so chapafupi. Matigari anali atagwira geti lolowera kumene 72