Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 67
Matigari
Gawo 11
Pa nthawiyi n’kuti chithunzithunzi chitatalika chifukwa dzu-
wa linali litatsika ndithu. Komabe, kunja kunkatenthabe kwam-
biri. Udzu unali utafota ndipo nawonso masamba a mitengo
ankaoneka kuti atoperatu kuwaulidwa ndi dzuwa. Mpweya
womwe unali patsikulo unali wa bee, ndipo pamsewu waphula
pankakhala ngati pamwamba pa uvuni yomwe yangowotched-
wa kumene. Ukamauonera patali nsewuwo, unkachita kuoneka
ukutulutsa m’bebe. Kupatulapo phokoso la galimoto zomwe
zinkayenda mumsewuwo komanso kulira kwa mbalame m’mi-
tengo, kunja kunangoti zii ngati kulibe anthu. Kunalibiretu
mphepo. Sikunkamveka phokoso la masamba komanso
m’makuka onse omwe anawadutsa, palibe khomo limene pa-
nayanikidwa zovala.
Posakhalitsa anakumana ndi malole atatu odzadza ndi
asilikali komanso ma Land-Rover anayi a apolisi. Asilikaliwo
anali atanyamula mifuti komanso zida zina zankhondo. Ko-
manso wapolisi aliyense anali atanyamula chamboko, chishango
komanso chovala chodzitetezera ku mpweya wokhetsa misozi.
“Kodi akulowera kuti awa?” Anafunsa Matigari.
“Akupita kufakitale,” anayankha Guthera. “Pajatu ogwira
ntchito kufakitale ananena kuti ayamba kunyanyala ntchito
kuyambira 2 koloko masana a lero.”
“Ndiye akupita kukamenyana ndi ogwira ntchitowo kapena
bwanji?” Matigari anafunsa.
“Bamboyutu wakhala zaka zambiri m’tchire.” Guthera anad-
ziuza mumtima mwake. “Akufunika kupita kaye kunyumba
n’kukapha tulo komanso kutopa konse komwe wakhala
akusungira zaka zomwe wakhala m’tchire. Ndi ndani m’dziko
66