Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 65

Matigari yachipambano mumtima mwanga: Nyum ba ija nd i yanga tsopano. Ndi ya ine komanso banja langa . . . N’chifukwa chaketu ndikufunafuna anthu a m’banja langa, ana anga aamuna ndi aakazi, azilamu komanso apongozi anga, azikazi anga . . .” “Ngakhalenso azikazi anu? N’chifukwa chiyani munawasi- ya?” Guthera anafunsa mokhala ngati akukayikira zoti mutu wa Matigari umagwira. Iye ankadzifunsa kuti, “N’chifukwa chiyani akuyankhula zopanda nzeruzi?” “Nanga ndinakawasiya kuti mwana wanga? N’chifukwa chaketu ndinatenga zida n’kuthawira kunkhalango komanso ku- mapiri kuti ndikamenye nkhondo n’cholinga choti nawonso akhale ndi nyumba. Koma pali vuto, kodi ndikawapeza kuti tsopano? Ndiyambira pati kuwafunafuna?” “Kodi munapita kuminda ya tiyi komanso khofi?” Guthera anafunsa akuoneka kuti akuchita manyazi chifukwa chokayikira kuti mutu wa Matigari umagwira. Iye anali atakumbukiranso kuti Matigari ndi amene anamupulumutsa kuchokera m’kamwa mwa galu wolusa uja. “Zoona mpaka pano adakagwirabe ntchito ngati akapolo m’minda ya tiyi?” anafunsa Matigari. “Nanga mumafuna kuti azitani? Masiku ano palibe malo om- we simungapeze azimayi akugwira ntchito kuti apeze kangache- pe koti akagulire chakudya cha ana komanso azimuna awo,” Guthera anatero, “Azimayi ambiri amagwira ntchito m’minda ya tiyi, khofi komanso gonje. Ngati mukufuna kupeza azikazi anu, koyambira kwabwino kungakhale kuminda imeneyi. Pitani mukayambe ndi kupulumutsa amenewo, musadandaule za ife chifukwa moyo wathu unatayika kalekale m’mabala muku- waonawa.” 64