Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 50

Matigari “Kodi sukuona kuti ndine wamsinkhu wofanana ndi bambo ako?” Matigari anauza Guthera pamene anapeza kampata ko- yankhula. “Tachoka pamiyendo pangapa msanga!” ananena zimenezi akumukankha. Kenako Guthera anakhala pakati pa Matigari ndi Muriuki. “Kodi mwakhala muli kuti bambo inu? Kodi mwachokera kumwezi, m’mlengalenga kapena? Kapena mukungofuna muy- erekedwe kaye? Taimani ndikuuzeni: Masiku anotu sitikusama- la za aliyense. Kaya ndi bambo ako, mwana wako, kaya ndi mchimwene wako kapena mchemwali wako, tilibe nazo ntchito. Nkhani yofunika kwambiri ndi makobidi basi. Ngakhale mwa- na ngati uyu ali apayu, ndikhoza kumuchengetera bwinobwino mpaka kumuiwalitsa kwawo. Eti ukuganiza bwanji mchim- wene? Anthu okhawo amene ndinalumbira kuti sindidzayereke- za kuchita nawo uhule ndi apolisi. Kapena nanunso ndinu wap- olisitu? Dzina lanu ndi ndani?” Matigari asanayankhe, Guthera anayang’ana chakuzenera ndipo anaona apolisi anali ndi galu aja. Anadzidzimuka kwam- biri atawaona moti anangoti balamanthu n’kuimirira. “Kalanga ine! Afisi awiri aja akubwera kuno . . . Sindikufuna kuti zitsiru zimenezi zindipusitse. Musachoke bambo, mundidi- kire pomwepa. Ndikubwera posachedwapa. Ndikabwera mudzandigulira umodzi eti?” Kenako Guthera anatuluka panja. Matigari anagwira chibwano chake mokhumudwa kwambiri akuganizira zimene zinachitikazo. Ankakhala ngati waikira mu- tu wake jeke. Mutu wake womwe unayamba kumulemera. Pachipumi pake panali patathethekanso mizere yatsinya la ukalamba. Tsinyalo linakula kwambiri moti linkangokhala ngati 49