Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 34

Matigari Gawo 7 “Nanga ndiwe ndani mwana wanga?” bamboyo anafunsa. “Ndani, mukunena ineyo?” munthuyo anayankha motero. “Dzina langa ndi Ngaruro wa Kiriro.” “Ngaruro? Wa m’banja la Kiriro? Zikomo kwambiri. Tsiku lina tizadziwana bwinobwino pa nthawi imene tidzasiye kuponyana miyala. Kodi ndi kuti kumene tingapeze malo oti tibisale dzuwa likuwirimali? Mukudziwa malo aliwonse abwino komwe tingaguleko chakudya cha ine ndi . . . ” “Muriuki. Dzina langa ndi Muriuki.” “Inde, malo omwe ine ndi Muriuki tingaguleko chakudya?” Kenako anamutembenukira n’kumufunsa kuti, “Kapena ukufuna kubwerera kumudzi wanu?” Muriuki anakayikira. Iye ankaona kuti bamboyo wavulala kwambiri moti sankafuna kungomusiya yekha. Komanso nanga akanamusiya bwanji atamva zoti akufuna kugula chakudya? “Aa, kaya!” mwanayo anayankha. “Ngati nditabwerera, mnyamata anandimenya uja akandimenyanso. Akhozanso kukandilanda zinthu zanga. Amakonda kumenya anzake amene uja. Komanso anyamata ena aja akandilanga chifukwa chokutengani inuyo, munthu woti sindikumudziwa, n’kukupititsani kumudzi wathu. Akhozanso kukandimenya chifukwa chokulolani kuti mudutse malire olowera m’mudzi wathu. Zingakhale bwino nditapanda kupitako kwa masiku awiri kapena atatu kuti aiwale kaye za nkhaniyi.” “Kodi nawenso umakhala m’mudzi wa ana uja?” Ngaruro anafunsa. “Inde, ndimakhala komweko,” mwanayo anayankha motero. 33