Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 244
Matigari
"Yesu Khristu? Ambuye yemwe adzabweretse Yerusalemu
watsopano padziko lapansi pano?" wina anawonjezera.
Matigari anakaikira kwa kanthawi. Kenako anayang'ana ana
aja mowamvera chisoni. Ndiyeno anaponya maso ake
chakutsogolo n'kumayang'ana ziphapha za magalimoto zija.
"Ayi," Matigari anayankha. "Mulungu amene analo-
seredwayo ali mwa inuyo, mwa ine komanso mwa anthu ena on-
se. Iye wakhala ali mwa ife kuchokera pachiyambi pa
chilengedwe. Olamulira opondereza akhala akufuna kupha
Mulungu ameneyo mwa ife. Koma tsiku lina Mulungu ameneyo
adzauka kwa akufa. Tsiku lina Mulungu ameneyo adzabwera
n'kudzatipulumutsa tonse amene timamukhulupirira.
Ndikunenazi sintchetera ayi."
"Iye adzabwera patsiku limene otsatira ake adzathe kuima
pamodzi popanda kuyang'ana fuko, mtundu kapena khungu ko-
manso pamene onse adzagwirizana kuchita chimodzi. Khama
lathu linatulutsa chuma chonse chili m'dziko muno. Choncho
kuyambira lero tikukana kumagona pamtetete n'kumakupu-
lidwa ndi mphepo. Tikukana kumayenda titavala masanza ko-
manso kumagona nayo njala. Dzikoli likufunika libwerere kwa
eni ake. Nthaka ibwerere kwa mlimi, mafakitale kwa ogwira
ntchito . . . Koma Mulungu ameneyo amakhala kwambiri mwa
inu ana a mādziko muno. Ndiye ngati mutalola kuti dzikoli lipite
kwa olamulira ankhanza komanso zidole zawo zomwe zim-
awateteza, ndiye kuti mukupha nokha Mulungu ali mwa inuyo.
N'chimodzimodzi kuchititsa kuti asaukitsidwe. Mulungu
ameneyo adzabweranso kokha ngati mutamulola kuti abwere."
Ana aja anayamba kuyang'anizana modabwa. Mawu a Matig-
ari ankasinthasintha, koma zimene ananenazo zinawagwira mti-
ma.
243