Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 236
Matigari
chopuma, kenako n'kuyamba kuuluka ngati ndege kapena
kuthamanga ngati hatchi. Iyeyo ankadziona ali pachiwongole-
ro n’kumayendetsa. Naye Matigari ankaphika mapulani a
mmene angapitire kukatenga zida zake kuti akatengenso
nyumba yake. Mawu amene ankayendayenda m’mutu mwake
anali akuti, ‘Mbewu imodzi ikalephera kumera sizichititsa mli-
mi kuti asiye kudzala.’ Guthera nayenso sanasiye kuganizira
za mzimayi uja. Iye ankamumvera chisoni kwambiri. Ankadzi-
uza kuti, ‘Azimayife ndiye tili pamavuto aakulu! Kulikonse
kumene tingalowere timakumana nazo zokhoma! Mzimayi uja
akapita kwawo, mwamuna wake akamuthibula, ndipo akamu-
funsa kuti anapezeka bwanji ndi mwamuna ali mbulanda
m’chipululu. Nayenso bwenzi lakelolo likapita kwawo, likati-
dzimula mkazi wake chifukwa wafunsa zoti amatani ndi mzi-
mayi awiriwiri m’chipululu.
Kenako Matigari anatsegula wailesi. M'galimotomo mu-
nayamba kumveka nyimbo zapansipansi ndipo kenako inafika
nthawi ya nkhani.
. . . Boma la USA lakana pempho la boma la Soviet Union kuti
padzikoli pachotsedwe zida zonse zanyukiliya* . . . Boma la USA lag-
aniza zoyamba kusunga zida m'mlengalenga . . . Boma la USA ko-
manso Soviet Union layamba kutumiza anthu enanso kuti apite kum-
wezi . . .
*Zimenezi zinalembedwa mu 1983, patadutsa zaka zingapo pambuyo pa
msonkhano wa ku Reykjavik.
"Anthu ake amangokhalira kulengeza nkhani zokhudza
dziko la USA komanso Soviet Union! Amangobwereza nkhani
zomwezomwezo mpaka zifike potinyansa. Kaya siz-
imawatopetsa?" Anatero Guthera.
235