Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 200

Matigari Anthu aja anapitirizabe kuimba mosaleletseka. Posakhalitsa apolisi anayambanso kuliza mizinga. "Msonkhanowu wathera pamenepa!" nduna ija inatero. "Zipitani m'makwanu! Nonse mukhoza kumapita m'makwanu tsopano!" "Pasapezeke munthu woima penapake! Komanso simukulo- ledwa kumayenda m'magulu a anthu oposa asanu," wapolisi uja anawonjezera. Koma pa nthawiyi n'kuti anthu aja akuimba mokweza kwambiri kuposa poyamba paja. Ena anayamba kukuwa kuti akufuna kuti Ngaruro wa Kiriro amasulidwe. Ena ankanena mawu akuti, "Atuluke m'boma anthu onse akuba komanso abodza!" "Ndaletsanso kuti anthu asamapezeke ali m'magulu m'mi- dzimu," bwanamkubwa uja anatero. "Ndalamula mafumu onse kuti agwiritsire ntchito mphamvu zomwe anapatsidwa ndi lamulo la Chiefs Act. Ndikuwapatsa mphamvu zoti akhoza ku- manga munthu aliyense amene apezeke akuyendayenda m'mudzi popanda sababu.*" *Sababu (Kiswahili): Kutanthauza popanda chifukwa. Anthu aja anaimirira n'kuyamba kuimba molowera komwe kunali ndunayo akuimba ngati akunena kuti akufuna kupita ku- chipinda anatsekera Matigari ma Njiruungi, Ngaruro wa Kiriro komanso anthu ena anapalamula milandu yokhudzana ndi ndale aja kuti akawatulutse. Mkulu wa apolisi uja analiza wizilo. Nthawi yomweyo apoli- si komanso asilikali aja anayamba kuthamangitsa anthu aja n'kumawamenya ndi matabwa a mfuti zawo. Anthu anayamba 199