Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 190

Matigari ntchito. Karl Marx ameneyu akusokoneza ophunzira, aphunzitsi komanso ogwira ntchito athu. Mabuku komanso zinthu za anthu amenewa ziyenera kuletsedwa kotheratu m’dziko muno. Ndikunena kuti mabuku komanso zinthu zina za Karl Marx, Lenin komanso Mao zisadzapezekenso m’dziko lathu lino.” Kenako anaimba mavesi awiri m’buku la Songs o f a Parro t n’kukhala pansi. Tsopano phungu wa kunyumba yamalamulo anaimirira. Iye anavala suti yoterela, taye yokhala ndi zilembo zija za KKK komanso magalasi a dzuwa aakulu mosagwirizana ndi mutu wake. Asanayambe kuyankhula anaimba kaye mavesi awiri m’buku lija la So ngs o f a Parro t. Kenako anayamba kuyankhula. “Ndikufuna kuphera mphongo zimene anzanga anena kale. Koma ndikufunanso kuwonjezera mfundo imodzi. Mfundo yake ndi yonena za Matigari ma Njiruungi. Ndamva zoti azimayi ena akumanena zoti abereka a Matigari ma Njiruungi ambiri. Kodi mwazerezeka naye kale Matigari ma Njiruungiyu? Boma la KKK lakhala likunena kuti gwero la umphawi womwe uli m’dziko muno ndi loti azimayi akumabereka ana ngati makoswe! Ngakhale m’nthawi ya atsamunda pamene ndinkagwira ntchito m’dipatimenti ya Co m m unity and Social Welfare, ankatiuza kuti kukhala ndi ana ambiri si kwabwino. Anthu ayenera kumakhala ndi ana mogwirizana ndi mmene m’thumba mwawo mulili. Amene alibe ndalama asamadzivutitse n’kumabereka ana. Ndipempha boma la USA kuti litsegule chipatala chaulere kuti azimayi azikatseketsa kumeneko. Anthu osauka ayenera kusiya kubereka ana! Ayenera kusiyira udindo umenewu anthu olemera. Mwaona, zikanakhala kuti anthu sakubereka ana ambirimbiri, sipakanakhala mikangano ya pakati pa ogwira ntchito ndi owalemba ntchito pankhani ya malipiro. 189