Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 183
Matigari
ufulu wa dziko lathu abweranso kuti adzatenge zinthu zawo!’
Mkulu wa apolisi uja ankayang’anabe Matigari mwachidwi
kwambiri. Maso ake anangoti ga pamanja a Matigari.
Mwapang’onopang’ono komanso mochenjera kwambiri,
anapititsa dzanja lake m’chiuno. Kenako mosaonetsera
anayamba kumasula kachikwama komwe anaikamo mfuti yake.
Nduna ija inati, “Oh . . . Ndiwe Matigari ma Njiruungi!
Bwera kutsogolo kuno! Bwera kuti tikuone bwinobwino.”
Apolisi ena anayamba kutsatira pang’onopang’ono Matigari.
Koma Matigari anawaopseza ponena kuti, “Musayerekeza
kundigwira! Ndiyenda ndekha, mapazi ndili nawo.”
Anthu omwe anakhala mopanikizana m’holoyo anayamba
kufutuka n’kumapereka njira kwa Matigari. Alendo onse anali
kutsogolo aja analinso ndi maganizo ofanana ndi omwe mkulu
wa apolisi uja anali nawo, oti Matigari ali ndi mfuti. Onse
anangoti maso ga pamanja a Matigari. Milomo ya wansembe uja
inayamba kugwedezeka ndipo zikuoneka kuti ankapereka
pemphero lachinunu.
Pamene Matigari ankayandikira kutsogolo, mkulu wa apolisi
uja anasolola mofulumira mfuti yake kuchoka m’kachikwama
kaja ndipo anamulozetsa Matigari, akukuwa kuti, “Manja
m’mwamba!”
Matigari anachotsa manja ake aja m’matumba akumwetulira,
ndipo anazindikira chifukwa chake mkulu wa apolisiyo anali
ndi mantha osaneneka. Kenako ananena kuti, “Musandiope, ine
ndadzimanga ndi lamba wamtendere.”
Koma mkulu wa apolisiyo anali asanakhutirebe kuti
Matigari alibe mfuti. Kenako anapereka chizindikiro kwa apolisi
awiri kuti akamuseche.
182