Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 158
Matigari
“Koma mvetserani kaye pang’ono. Ndife odala m’dziko mu-
no chifukwa mtsogoleri wathu, Pulezidenti Ole, ndi munthu
woopa Mulungu komanso ndi Mkhristu. Ndi munthunso woona
patali kwambiri. Iye ali ndi unduna womwe umaona nkhani ya
choonadi ndi chilungamo. Nayonso Nduna Yoona Zachilunga-
mo, monga amachitira apulezidenti athu, sijomba kutchalitchi.
Ndunayi ikubwera kudzayendera anthu a m’dera lino. Monga
mukudziwira, amakonda kupita m’madera osiyanasiyana
n’kumauza anthu kuti amayesetsa kuonetsetsa kuti chilungamo
chikuchitika komanso kuti m’dziko muno muli bata ndi mtende-
re. Mwachitsanzo, akhala akuchititsa msonkhano madzulo ano
muholo yaikulu ya m’tauni muno. Akufuna kukonza mavuto
omwe akuchititsa kuti ogwira ntchito azipanga masitiraka. Pilizi
chonde, pitani kwa Nduna Yoona Zachilungamo n’kukaifunsa
kuti: Kodi ndi kuti kumene munthu angapeze choonadi ndi chi-
lungamo m’dzikoli?”
157