Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 143

Matigari chaperekedwa pawailesi lero? Ophunzira asanu a pasukulu ya ukachenjede agamulidwa kuti akakhale kundende yachitetezo chokhwima kwa zaka zisanu. Koma si zokhazo . . . ” Wophunzirayo anayankhula mokayikira. Iye anali wokhu- mudwa kwambiri. Pamene ankayankhula mawu ake ankamveka ndi misozi ya zaka zambiri. “Kodi tasiyana liti? Kodi si madzulo a dzulo laliwisiri? Kapena ndi dzana? Kaya ndiliti kaya. Kaya ndi dzulo, dzana, kaya chaka chatha, zinthu zakhala zikuchitika chimodzimodzi. Sizikusinthayi. Ndinathawira kusukulu kuti ndikabisale pakati pa anzanga. Ndinamva zoti aitanitsa msonkhano woti apempherere anzawo amene amangidwa. Amafunanso kuti apempherere mtendere komanso chikondi m’dziko muno. Oh! Mukudziwa zimene tinakumana nazo ku- meneko? Tinakumana ndi tsoka lofanana ndi limene ogwira ntchito pafakitale aja anakumana nalo. Pamene timagwada kuti tiyambe kugwa nalo pemphero, titatseka m’maso, tinangozindikira kuti asilikali ndi apolisi atizungulira. Ophunzi- ra atubulidwa koopsa moti ena awathyola dziboda. Ophunzira makumi awiri ndi asanu anaphedwa nthawi yomweyo. Mtsi- kana m’modzi anali woyembekezera ndi mimba ya miyezi isanu ndi itatu . . . Anamumenya moti wapita padera. Koma ayi ndithu dzikoli latembenukadi! Kodi zonsezi, zonse zimene zachitikazi zalengezedwa pawailesi paja, pa Wailesi ya Choonadi yadya waniyi? Ayi! Zimene alengeza ndi zoti sukulu yaukachenjedeyo yatsekedwa chifukwa ophunzira anachita sitiraka chifukwa sa- kupatsidwa chakudya chabwino.” “Limenelotu ndi bodza lankunkhuniza! Ineyo, ineine, ndinali komweko! Ndine mboni pankhaniyi. Ndangopulumukira pa- kangaude n’kuthawa kubwera kuno. Koma ndaphunzirapo zin- thu zingapo. Pulezidenti Ole sakusewera ndi munthu. 142