Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 134

Matigari lachenjeza kuti silinyengerera chipembedzo chilichonse chomwe chinga- pitirize kufalitsa mphekesera yakuti Yesu wabweranso. Lachenjezanso kuti lilanda malaisesi kwa eni matatu* onse omwe angalole kuti nkhani zimenezi zizikambidwa m'magalimoto awo. Aliyense ayenera kudziwa kuti amenewa ndi aneneri onyenga. Sizingatheke kuti Yesu abwere m’dziko muno asanakambirane kaye ndi mtsogoleri wadziko lino, Pulezidenti Ole. Aliyense akulimbikitsidwa kukanena kupolisi ngati at- amva munthu wina akunena kuti iyeyo ndi Yesu kapena Gabrieli. *Matatu: Mawuwa poyamba ankagwiritsidwa ntchito ponena za magalimoto oyenda popan- da chilolezo. Koma pano amangonena za magalimoto amatola onse komanso mabasi omwe mumadzadza anthu ndipo nthawi zambiri anthu amakambirana nkhani zosiyanasiyana zomwe zangochitika kumene kuphatikizaponso mabodza. Gawo 10 Wofunafuna choonadi ndi chilungamo anataya mtima. Koma wofufuza chilungamo weniweni satopa ngakhale nsapato zake zitatha ndi kuyenda. Mlimi sasiya kudzala mbewu kokha chifu- kwa choti mbewu ina sikumera. Kuti munthu apindule amafu- nika kukhala wolimbika komanso safunika kutopa ndi kugogo- da. Choonadi chiyenera kufufuza chilungamo. Chilungamo chiyenera kufufuza choonadi. Chilungamo chikapambana, choonadi chimalamulira dziko. 133