Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Página 109
Matigari
Gawo 1
Ana a kumanda a galimoto aja atangodzuka tsiku lotsatira,
anapeza Muriuki akugona mu Mercedes-Benz yake ndipo
anamudzutsa n’kukhala momuzungulira.
“Kodi wabwera nthawi yanji?”
“Usiku?”
“Tatiuze . . . tatiuze za Matigari ma Njiruungi.”
Mphepo ya nkhani ya mmene Matigari anapulumutsira
Guthera inali itawapeza kale. Iwo anamva mmene apolisi
anachitira mantha pamene Matigari ankawayankhula. Wap-
olisiyo anali yemwe uja ankangokhalira kuwazunza kwa zaka
zambiri. Anawa ankadziimba mlandu kwambiri. Iwo ankadzi-
funsa kuti: ‘N’chifukwa chiyani tinagenda munthu wabwino
ngati ameneyu? Kodi Muriuki ali kuti atifotokozere za munthu
ameneyu?’ N’chifukwa chaketu anadzukirira m’mawa n’kupita
kukakumana ndi Muriuki.
Naye Muriuki anawonjezera thendo munkhaniyi. Anyama-
tawo anagoma zedi ndi zimene anawafotokozera. Iwo ankafun-
sa kuti: ‘N’zoona kuti anamangidwa? N’zoona kuti zitseko za
ndende zinawatsegukira modabwitsa? Kodi nkhani imeneyi
ailengeza pawailesi?’
Nthawi yomweyo mwana wina anathamanga kukatenga
wailesi yomwe anaitola kumtaya ija. Anawo anagwirizana kuti
wailesiyo ikhala ya mudzi wonse n’cholinga choti azidziwa
zomwe zikuchitika m’dziko. Iwo anapereka ndalama ya chipu-
kutamisozi kwa mwana amene anatola wailesiyo. Anawa anka-
tenga wailesiyi kulikonse komwe ankalowera.
Onse anasonkhana malo amodzi mozungulira wailesiyo
n’kumamvetsera nkhani. Iwo ankafuna kumva zokhudza
108